NYIMBO 107
Tizitsanzira Chikondi cha Mulungu
-
1. Yehova M’lungu n’chitsanzo chabwino,
Inde cha chikondi.
Zochita zake zimatithandiza
Kuti tizimutsanzira.
Anatipatsa mwana wake Yesu
Kuti tikhululukidwe zolakwa.
Ndi umbonidi wa chikondi chake.
M’lungu wathu ndi chikondidi.
-
2. Timasonyeza chikondi choona
Potsanzira M’lungu.
Abale onse timawathandiza
Mosasankha aliyense.
Chikondi chingakhale chenicheni
Ngati timakonda M’lungu ndi anthu.
Tizikwirira zolakwa za ena,
Chimenechi ndicho chikondi.
-
3. Chikondi chathu chimatithandiza
Kumagwirizana.
Atate wathu akufuna kuti
Tidzalawe mgwirizano.
Timapeza chikondi chenicheni
Ndipo n’chomwe chimatidziwikitsa.
Abale athu amatikumbutsa
Za chikondi cha M’lungu wathu.
(Onaninso Aroma 12:10; Aef. 4:3; 2 Pet. 1:7.)