NYIMBO 62
Nyimbo Yatsopano
-
1. Imbira M’lungu, imba nyimbo yatsopano.
Unene kwa onse ntchito zake zonse.
Umutamande, Mulungu ndi wopambana.
Ndi wachilungamo
Poweruza anthu.
(KOLASI)
Imbani
Nyimbo yatsopano.
Imbani,
Yehova ndi Mfumu.
-
2. Mosangalala fuula kwa Mfumu yathu.
Muzimutamanda ndi nyimbo yokoma.
Tiyeni tonse timuimbire mokweza.
Zeze ndi lipenga
Ziimbe pamodzi.
(KOLASI)
Imbani
Nyimbo yatsopano.
Imbani,
Yehova ndi Mfumu.
-
3. Nyanja ndi zonse mmenemo zimutamande.
Zolengedwa zake zizimutamanda.
Dziko lapansi nalonso limutamande.
Mapiri ndi zigwa
Zimutamandenso.
(KOLASI)
Imbani
Nyimbo yatsopano.
Imbani,
Yehova ndi Mfumu.
(Onaninso Sal. 96:1; 149:1; Yes. 42:10.)