Pitani ku nkhani yake

Kodi M’Baibulo Mungapezeke Mawu Omwe Angandilimbikitse?

Kodi M’Baibulo Mungapezeke Mawu Omwe Angandilimbikitse?

Yankho la m’Baibulo

 Inde. (Aroma 15:4) Mwachitsanzo, taonani mfundo za m’Baibulo zomwe zili m’munsimu zomwe zathandiza anthu ambiri omwe akulimbana ndi mavuto komanso nkhawa zosiyanasiyana.

Zimene zili munkhaniyi

 Mavuto

 Salimo 23:4: “Ngakhale ndikuyenda m’chigwa cha mdima wandiweyani, sindikuopa kanthu, pakuti inu muli ndi ine.”

 Mfundo yake: Tikamapemphera kwa Mulungu komanso kudalira Mawu ake opezeka m’Baibulo kuti atitsogolere, tikhoza kulimbana ndi mavuto athu.

 Afilipi 4:13: “Pa zinthu zonse, ndimapeza mphamvu kuchokera kwa iye amene amandipatsa mphamvu.”

 Mfundo yake: Mulungu akhoza kutipatsa mphamvu kuti tilimbane ndi vuto lililonse.

 Imfa ya munthu amene tinkamukonda

 Mlaliki 9:10: “Kulibe kugwira ntchito, kuganiza zochita, kudziwa zinthu, kapena nzeru, ku Manda kumene ukupitako.”

 Mfundo yake: Anthu omwe anamwalira sakuvutika ndipo sangativulaze chifukwa sadziwa chilichonse.

 Machitidwe 24:15: “Kudzakhala kuuka.”

 Mfundo yake: Mulungu ali ndi mphamvu zodzaukitsa omwe anamwalira kuti adzakhalenso ndi moyo.

 Kudziimba mlandu

 Salimo 86:5: “Inu Yehova  a ndinu Mulungu wabwino ndipo ndinu wokonzeka kukhululuka. Kukoma mtima kosatha kumene mumawasonyeza onse oitana pa inu ndi kwakukulu.”

 Mfundo yake: Mulungu amakhululukira anthu omwe amadzimvera chisoni chifukwa cha zinthu zomwe analakwitsa ndiponso omwe ndi ofunitsitsa kuti asadzabwerezenso zomwe anachita.

 Salimo 103:12: “Monga mmene kum’mawa kwatalikirana ndi kumadzulo, momwemonso, watiikira kutali zolakwa zathu.”

 Mfundo yake: Mulungu akatikhululukira, amatiikira kutali machimo athu. Ndipo sakhalira kutikumbutsa zomwe tinalakwa ndi cholinga chofuna kutiimba mlandu kapena kutilanga.

 Kukhumudwa

 Salimo 31:7: “Mwaona kusautsika kwanga. Mwadziwa zowawa zimene zandigwera.”

 Mfundo yake: Mulungu akudziwa bwino za mavuto omwe mukudutsamo. Amadziwanso bwino mmene mavutowo amakukhudzirani mumtima ngakhale pamene anthu ena sakuona zimenezo.

 Salimo 34:18: “Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka. Ndipo odzimvera chisoni mumtima mwawo amawapulumutsa.”

 Mfundo yake: Mulungu akulonjeza kuti ndi wokonzeka kukuthandizani pamene muli wokhumudwa. Iye angathe kukupatsani mphamvu kuti mupirire.

 Kudwala

 Salimo 41:3: “Yehova adzachirikiza wonyozekayo pamene akudwala pabedi lake.”

 Mfundo yake: Mulungu akhoza kukuthandizani pamene mukudwala kwambiri. Angachite zimenezi pokupatsani mtendere wamumtima, mphamvu zoti muthe kupirira komanso nzeru kuti mukwanitse kusankha bwino zoti muchite.

 Yesaya 33:24: “Palibe munthu wokhala m’dzikolo amene adzanene kuti: ‘Ndikudwala.’”

 Mfundo yake: Mulungu analonjeza kuti m’tsogolomu anthu onse adzakhala ndi moyo wathanzi.

 Nkhawa komanso kuvutika maganizo

 Salimo 94:19 “Malingaliro osautsa atandichulukira mumtima mwanga, Mawu anu otonthoza anayamba kusangalatsa moyo wanga.”

 Mfundo yake: Tikamadalira Yehova pamene tili ndi nkhawa, Iye angatithandize kuti tikhazikitse maganizo athu m’malo.

 1 Petulo 5:7: ‘Mutulireni nkhawa zanu zonse, pakuti amakuderani nkhawa.’

 Mfundo yake: Mulungu amatidera nkhawa tikamavutika. Iye amatilimbikitsa kuti tizipemphera kwa iye n’kumuuza zomwe zikutidetsa nkhawa.

 Nkhondo

 Salimo 46:9: “Akuletsa nkhondo mpaka kumalekezero a dziko lapansi.”

 Mfundo yake: Posachedwa, Ufumu wa Mulungu udzathetsa nkhondo zonse.

 Salimo 37:11, 29: “Anthu ofatsa adzalandira dziko lapansi, ndipo adzasangalala ndi mtendere wochuluka. . . . Olungama adzalandira dziko lapansi, ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya.”

 Mfundo yake: Anthu abwino adzakhala mwamtendere padziko lapansi mpaka kalekale.

 Kudera nkhawa zam’tsogolo

 Yeremiya 29:11: “Maganizo anga kwa inu ndikuwadziwa bwino. Ndikuganizira zokupatsani mtendere osati masoka, kuti mukhale ndi chiyembekezo chabwino ndiponso tsogolo labwino,’ watero Yehova.”

 Mfundo yake: Mulungu akutsimikizira anthu ake kuti adzawapatsa tsogolo labwino kwambiri.

 Chivumbulutso 21:4: “Adzapukuta misozi yonse m’maso mwawo, ndipo imfa sidzakhalaponso. Sipadzakhalanso kulira, kapena kubuula, ngakhale kupweteka. Zakalezo zapita.”

 Mfundo yake: Mulungu akulonjeza kuti adzachotsa zinthu zonse zoipa zomwe timaziona komanso kukumana nazo masiku ano.

a Yehova ndi dzina lenileni la Mulungu. (Salimo 83:18) Werengani nkhani yakuti, “Kodi Yehova Ndi Ndani?