Pitani ku nkhani yake

Pitani ku mitu ya nkhani

FUNSO 3

Kodi ndi Ndani Amene Analemba Baibulo?

“Mose analemba mawu onse a Yehova.”

Ekisodo 24:4

“Danieli analota maloto ndipo anaona masomphenya atagona pabedi lake. Ndiyeno analemba zimene analotazo ndipo anafotokoza nkhani yonseyo.”

Danieli 7:1

“Pamene munalandira mawu a Mulungu amene munamva kwa ife, simunawalandire monga mawu a anthu, koma mmene alilidi, monga mawu a Mulungu.”

1 Atesalonika 2:​13

“Malemba onse anauziridwa ndi Mulungu, ndipo ndi othandiza pophunzitsa.”

2 Timoteyo 3:​16

“Ulosi sunachokere kwa anthu, koma anthuwo analankhula mawu ochokera kwa Mulungu motsogoleredwa ndi mzimu woyera.”

2 Petulo 1:​21