NYIMBO 12
Yehova Mulungu Wamkulu
-
1. Inu Yehova M’lungu Wamkulu,
Wabwino m’zinthu zonse,
Tizikutamandani.
Muli ndi mphamvu, chikondi, nzeru.
Mulungu wathu ndinu.
-
2. Tikumaona chifundo chanu.
Ngakhale ndife fumbi
Tikapempha mumamva.
Mumatidyetsa, kutiphunzitsa,
Mumatithandizadi.
-
3. Tikutamanda inu Yehova.
Tikukuimbirani
Mosangalala ndithu.
Muyeneradi kutamandidwa
Kuchokera mumtima.
(Onaninso Deut. 32:4; Miy. 16:12; Mat. 6:10; Chiv. 4:11.)