NYIMBO 134
Ana Ndi Mphatso Yochokera kwa Mulungu
-
1. Mwamuna ndi mkazi wake
Akalandira mphatso ya mwana,
Ayenera kukumbukira
Mwanayo si wawo okha.
Ndi mphatso yochoka kwa M’lungu.
Amapatsa chikondi ndi moyo.
Amapereka malangizo
Othandizadi kwa makolo.
(KOLASI)
Mphatsoyi ndi yopatulika
Ndipo muisamalire.
Muphunzitseni choonadi
Ndipo mudzamuthandiza.
-
2. Mawu onse a Mulungu
Azikhalatu mumtima mwanu.
Muziuzanso ana anu,
Uwu ndi udindo wanu.
Muziwaphunzitsa poyenda,
Podzuka ndi pa nthawi yopuma.
Akamakula saiwala.
Azilandira madalitso.
(KOLASI)
Mphatsoyi ndi yopatulika
Ndipo muisamalire.
Muphunzitseni choonadi
Ndipo mudzamuthandiza.
(Onaninso Deut. 6:6, 7; Aef. 6:4; 1 Tim. 4:16.)