Wolembedwa ndi Mateyu 12:1-50

  • Yesu ndi “Mbuye wa Sabata” (1-8)

  • Anachiritsa munthu wolumala dzanja (9-14)

  • Mtumiki amene Mulungu amamukonda (15-21)

  • Anatulutsa ziwanda pogwiritsa ntchito mzimu woyera (22-30)

  • Tchimo losakhululukidwa (31, 32)

  • Mtengo umadziwika ndi zipatso zake (33-37)

  • Chizindikiro cha Yona (38-42)

  • Mzimu wonyansa ukabwerera (43-45)

  • Amayi ake a Yesu komanso azichimwene ake (46-50)

12  Pa nthawi ina, Yesu ankadutsa mʼminda ya tirigu pa tsiku la Sabata. Ophunzira ake anamva njala ndipo anayamba kubudula ngala za tirigu nʼkumadya.+  Afarisi ataona zimenezi anamuuza kuti: “Taona! Ophunzira ako akuchita zinthu zimene ndi zosayenera kuchita pa Sabata.”+  Koma iye anawayankha kuti: “Kodi simunawerenge zimene Davide anachita, iyeyo ndi amuna omwe anali naye atamva njala?+  Iye analowa mʼnyumba ya Mulungu ndipo anadya mitanda ya mkate woonetsa kwa Mulungu,*+ umene iye ndi anthu omwe anali nawo aja sankayenera kudya malinga ndi malamulo, koma ansembe okha.+  Kapena kodi simunawerenge mʼChilamulo kuti ansembe mʼkachisi ankaphwanya Sabata pogwira ntchito tsiku la Sabata koma nʼkukhalabe osalakwa?+  Koma ndikukuuzani kuti winawake wamkulu kuposa kachisi ali pano.+  Komabe, ngati mukanamvetsa tanthauzo la mawu akuti, ‘Ndikufuna chifundo+ osati nsembe,’+ simukanaweruza anthu osalakwa.  Chifukwa Mwana wa munthu ndi Mbuye wa Sabata.”+  Atachoka malo amenewo, anakalowa musunagoge wawo. 10  Mmenemo munali munthu wolumala dzanja.+ Choncho iwo anamufunsa kuti, “Kodi nʼzololeka kuchiritsa odwala pa tsiku la Sabata?” Cholinga chawo chinali choti amupezere chifukwa nʼkumuimba mlandu.+ 11  Koma iye anawayankha kuti: “Mutakhala ndi nkhosa imodzi yokha, ndiyeno nkhosayo nʼkugwera mʼdzenje pa tsiku la Sabata, kodi alipo pakati panu amene sangaigwire nʼkuitulutsa?+ 12  Komatu munthu ndi wofunika kwambiri kuposa nkhosa! Choncho ndi zololeka kuchita chinthu chabwino pa tsiku la Sabata.” 13  Kenako anauza munthuyo kuti: “Tambasula dzanja lako.” Iye analitambasuladi ndipo linakhalanso bwinobwino ngati linzake. 14  Koma Afarisiwo anatuluka nʼkukakonza chiwembu kuti amuphe. 15  Yesu atadziwa zimenezi, anachoka pamalo amenewo. Anthu ambiri anamutsatira+ ndipo iye anawachiritsa onsewo, 16  koma anawalamula mwamphamvu kuti asamuulule.+ 17  Anachita zimenezi kuti zimene Mulungu ananena kudzera mwa mneneri Yesaya zikwaniritsidwe. Iye ananena kuti: 18  “Taonani mtumiki wanga+ amene ndamusankha, wokondedwa wanga, amene amandisangalatsa kwambiri.+ Ndidzaika mzimu wanga pa iye+ ndipo anthu a mitundu ina adzawasonyeza bwinobwino chilungamo chenicheni. 19  Sadzakangana ndi munthu+ kapena kufuula ndipo palibe amene adzamve mawu ake mʼmisewu ikuluikulu. 20  Bango lophwanyika sadzalithyola ndipo chingwe cha nyale chimene chikufuka utsi sadzachizimitsa,+ mpaka atakwanitsa kubweretsa chilungamo. 21  Ndithudi, mʼdzina lake mitundu ya anthu idzayembekezera zabwino.”+ 22  Kenako anamubweretsera munthu wogwidwa ndi chiwanda, amenenso anali ndi vuto losaona komanso sankalankhula ndipo iye anamuchiritsa, moti munthu wosalankhulayo anayamba kulankhula ndiponso kuona. 23  Zitatero, gulu la anthulo linadabwa kwambiri ndipo anayamba kunena kuti: “Kodi ameneyu sangakhale Mwana wa Davide uja?” 24  Afarisi atamva zimenezi ananena kuti: “Ameneyutu sikuti amatulutsa ziwanda ndi mphamvu zake ayi koma ndi mphamvu za Belezebule,* wolamulira ziwanda.”+ 25  Atadziwa maganizo awo, iye anawauza kuti: “Ufumu uliwonse wogawanika umatha ndipo mzinda kapena nyumba iliyonse yogawanika sikhalitsa. 26  Mofanana ndi zimenezi, ngati Satana amatulutsa Satana, ndiye kuti wagawanika. Nanga tsopano ufumu wake ungakhalepo bwanji? 27  Komanso ngati ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu za Belezebule, nanga otsatira anu amazitulutsa ndi mphamvu za ndani? Nʼchifukwa chake otsatira anuwo adzakuweruzani kuti ndinu olakwa. 28  Koma ngati ine ndimatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya mzimu wa Mulungu, ndiye kuti Ufumu wa Mulungu wakufikirani modzidzimutsa.+ 29  Kapena munthu angalowe bwanji mʼnyumba ya munthu wamphamvu nʼkumulanda katundu wake, ngati choyamba atapanda kumanga munthu wamphamvuyo? Akatero mʼpamene angathe kutenga katundu mʼnyumbamo. 30  Aliyense amene sali kumbali yanga akutsutsana ndi ine ndipo amene sagwira ntchito yosonkhanitsa anthu limodzi ndi ine amawabalalitsa.+ 31  Pa chifukwa chimenechi ndikukuuzani kuti, anthu adzakhululukidwa tchimo la mtundu uliwonse ndi mawu aliwonse onyoza, koma wonyoza mzimu sadzakhululukidwa.+ 32  Mwachitsanzo, aliyense wolankhula mawu onyoza Mwana wa munthu, adzakhululukidwa.+ Koma aliyense wolankhula mawu onyoza mzimu woyera, sadzakhululukidwa, mʼnthawi* ino kapena ikubwerayo.+ 33  Inu mumachititsa kuti mtengo ndi zipatso zake zikhale zabwino kapena mumachititsa kuti mtengo ndi zipatso zake zikhale zovunda, chifukwa mtengo umadziwika ndi zipatso zake.+ 34  Ana a njoka inu,+ mungalankhule bwanji zinthu zabwino pamene muli oipa? Chifukwa pakamwa pamalankhula zosefukira mumtima.+ 35  Munthu wabwino amatulutsa zabwino mʼchuma chabwino chamumtima mwake, koma munthu woipa amatulutsa zoipa mʼchuma choipa chamumtima mwake.+ 36  Ndikukuuzani kuti pa Tsiku la Chiweruzo, anthu adzayankha mlandu+ pa mawu aliwonse opanda pake amene iwo amalankhula. 37  Chifukwa ndi mawu ako udzaweruzidwa kuti ndiwe wolungama ndipo ndi mawu akonso udzaweruzidwa kuti ndiwe wolakwa.” 38  Ndiyeno alembi ndi Afarisi ena anamupempha kuti: “Mphunzitsi, tikufuna mutionetse chizindikiro.”+ 39  Poyankha iye anawauza kuti: “Mʼbadwo woipa komanso wachigololo* ukufunitsitsa utaona chizindikiro. Koma sudzapatsidwa chizindikiro chilichonse kupatulapo chizindikiro cha mneneri Yona chokha.+ 40  Chifukwa mofanana ndi Yona amene anakhala mʼmimba mwa chinsomba chachikulu masiku atatu, masana ndi usiku,+ Mwana wa munthu nayenso adzakhala mumtima wa dziko lapansi masiku atatu, masana ndi usiku.+ 41  Anthu a ku Nineve adzauka pa Tsiku la Chiweruzo limodzi ndi mʼbadwo uwu ndipo adzautsutsa, chifukwa iwo analapa atamva ulaliki wa Yona.+ Koma tsopano wina woposa Yona ali pano.+ 42  Mfumukazi yakumʼmwera adzaiukitsa kwa akufa pa Tsiku la Chiweruzo limodzi ndi mʼbadwo uwu ndipo idzautsutsa, chifukwa mfumukazi imeneyi inabwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomo.+ Koma tsopano wina woposa Solomo ali pano.+ 43  Mzimu wonyansa ukatuluka mwa munthu, umadutsa mʼmalo opanda madzi kufunafuna malo okhala ndipo supeza aliwonse.+ 44  Ndiyeno umati, ‘Ndibwerera kunyumba yanga imene ndinatulukamo ija.’ Ukafika umapeza kuti simukukhala aliyense koma ndi mosesedwa bwino komanso mokongoletsedwa. 45  Ukatero umapita kukatenga mizimu ina 7 yoipa kwambiri kuposa umenewo ndipo ikalowa mkatimo imakhala mmenemo. Zotsatira zake, zochita za munthuyo zimakhala zoipa kwambiri kuposa poyamba.+ Ndi mmenenso zidzakhalire ndi mʼbadwo woipawu.” 46  Ali mkati molankhula ndi gulu la anthulo, kunabwera mayi ake ndi azichimwene ake.+ Iwo anaima panja ndipo ankafuna kuti alankhule naye.+ 47  Choncho munthu wina anamuuza kuti: “Mayi anu ndi azichimwene anu aima panjapa, akufuna kulankhula nanu.” 48  Poyankha iye anauza munthu amene ankalankhula nayeyo kuti: “Kodi mayi anga ndi ndani ndipo azichimwene anga ndi ndani?” 49  Kenako anatambasula dzanja lake ndi kuloza ophunzira ake, nʼkunena kuti: “Ona! Mayi anga ndi azichimwene anga ndi awa!+ 50  Chifukwa aliyense amene amachita zimene Atate wanga wakumwamba amafuna, ameneyo ndi mchimwene wanga, mchemwali wanga ndi mayi anga.”+

Mawu a M'munsi

Kapena kuti, “mkate wachionetsero.”
Dzina limene Satana, yemwe ndi kalonga kapena kuti wolamulira ziwanda amadziwika nalo.
Kapena kuti, “wosakhulupirika.”