Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Capamodzi Tidzamuimbila Mokondwa Yehova

Capamodzi Tidzamuimbila Mokondwa Yehova

Daunilodi

  1. 1. Anthu akulila,

    ambili asocela

    Pali nkhondo; kumenyana,

    Mayankho sapezeka

    Anthu amanama

    mwa kulonjeza bodza

    Koma Yehova akulonjeza

    Kutipatsa mtendele.

    (KOLASI)

    Tidzapeza

    mtendele

    Capamodzi

    tidzamuimbila

    Yehova mokondwa

  2. 2. Malonjezo onse

    adzakwanilitsidwa

    Yehova M’lungu amatikonda

    Tidzaona mtendele,

    Siticita mantha

    amatitonthoza

    Ndipo tidziŵa tidzapeza

    Mtendele wosatha.

    (KOLASI)

    Tidzapeza

    mtendele

    Capamodzi

    tidzamuimbila

    Yehova mokondwa.

    (BILIJI)

    M’dziko latsopano

    Tidzamasulidwa

    Sikudzakhala imfa cisoni

    Anthu adzamvela

    Yehova Mulungu.

    (KOLASI)

    Tidzapeza

    mtendele

    Capamodzi

    tidzamuimbila

    Tidzapeza

    mtendele

    Capamodzi

    tidzamuimbila

    Yehova mokondwa

    Ku’muyaya wonse!