Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Tsiku Iliyonse ili na Nkhawa Zake

Tsiku Iliyonse ili na Nkhawa Zake

Daunilodi:

  1. 1. Zonse zidzakhala bwino m’paradaiso,

    Nimaikhulupilila lonjezo ya M’lungu

    Koma n’covuta kuona madalitso a m’tsogolo

    Na cikondi ca Yehova pamene nivutika,

    Koma M’lungu alipo.

    (KOLASI)

    Nimapemphela kwa M’lungu,

    Pamene nkhawa zibwela

    Nimadalila iye.

    Nthawi zonse amayankha

    Kupitila mu Baibo

    Na mabwenzi abwino.

    Tsiku iliyonse i’na nkhawa.

    Ine sinidela nkhawa

    Za mavuto ya kutsogolo

    Ni’na mtendele mu mtima wanga.

  2. 2. Mvela mawu anga mnzanga

    Dziŵa nikukonda.

    Ganizila zabwino osati pamavuto.

    Kumbuka, M’lungu wathu atipatsa mwana wake.

    Conco, iwe mudalile

    Safuna tizivutika

    Conco usayope.

    (KOLASI)

    Pemphela kwa M’lungu

    Pamene nkhawa zibwela

    Tizidalila iye.

    Nthawi zonse amayankha

    Kupitila mu Baibo

    Na mabwenzi abwino.

    Tsiku iliyonse i’na nkhawa

    Tisazidela nkhawa

    Za mavuto yakutsogolo

    Mitima yathu i’na mtendele.

    (KOLASI)

    Pemphela kwa M’lungu

    Pamene nkhawa zibwela

    Tizidalila iye.

    Nthawi zonse amayankha

    Kupitila mu Baibo

    Na mabwenzi abwino.

    Tsiku iliyonse i’na nkhawa

    Tisazidela nkhawa

    Za mavuto yakutsogolo

    Mitima yathu i’na mtendele

    Ti’na mtendele.